LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb19 January tsa. 7
  • “Paulo Anayamika Mulungu Ndipo Analimba Mtima”

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • “Paulo Anayamika Mulungu Ndipo Analimba Mtima”
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
  • Nkhani Zofanana
  • Amagwila Nchito Molimbika Potitumikila
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
  • Oyang’anila Oweta Nkhosa za Mulungu
    Gulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
  • Kodi Oyang’anila Dela Amatithandiza m’Njila Ziti?
    Ndani Amene Akucita Cifunilo Ca Yehova Masiku Ano?
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
mwb19 January tsa. 7
Paulo ayamika Mulungu cifukwa ca abale amene abwela kukamucingamila

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

“Paulo Anayamika Mulungu Ndipo Analimba Mtima”

Mpingo wa ku Roma utamva zakuti Paulo akubwela, abale osankhidwa anayenda mtunda wa makilomita 64 kuti akakumane naye. Kodi cikondi cimene iwo anaonetsa cinamukhudza bwanji Paulo? “Paulo atawaona, anayamika Mulungu, ndipo analimba mtima.” (Mac. 28:15) N’zoona kuti Paulo anali kudziŵika kuti anali kulimbikitsa mipingo imene anali kucezetsa. Koma apa, pamene anali mkaidi, ndiye analimbikitsidwa.—2 Akor. 13:10.

Masiku ano, oyang’anila madela amayendela mipingo kuti azilimbikitsa abale na alongo. Mofanana na anthu ena onse a Mulungu, nawonso nthawi zina amamvela kulema, amakhala na nkhawa, ndiponso zinthu zolefula. Conco, woyang’anila dela na mkazi wake akadzabwela kudzacezetsa mpingo wanu, mudzacitapo ciani kuti muwathandize kukhala olimba mtima, na kuti pakakhale ‘kulimbikitsana’?—Aroma 1:11, 12.

  • Woyang’anila dela atsogoza msonkhano wokonzekela ulaliki

    Muzipezeka pa kukumana kokonzekela ulaliki. Woyang’anila dela amalimbikitsidwa ngati ofalitsa amadzimana zina kuti acilikize mokwanila wiki yapadela. (1 Ates. 1:2, 3; 2:20) Mungaciteko upainiya wothandiza m’mwezi wa kucezetsa kwake. Kodi simungalembetseko kuti mukapite naye mu ulaliki pamodzi na mkazi wake, kapena kutengako mmodzi wa iwo na kupita naye ku phunzilo la Baibo? Iwo amakondwela kuseŵenza na ofalitsa osiyana-siyana, ngakhale acatsopano kapena amene alibe luso lolalikila.

  • Woyang’anila dela na mkazi wake alandilidwa bwino na banja lina

    Khalani oceleza. Kodi mungapelekeko malo ogona kwa woyang’anila dela kapena kumuitanila ku cakudya? Kucita izi, kudzaonetsa kuti muma’mkonda pamodzi na mkazi wake. Iwo sayembekezela zinthu zapamwamba.—Luka 10:38-42.

  • Woyang’anila dela atsogoza msonkhano wa akulu

    Muzimvela na kuseŵenzetsa malangizo na uphungu wake. Mwacikondi, woyang’anila dela amatithandiza kuona mbali zimene tifunika kuwongolela pocita utumiki wathu kwa Yehova. Nthawi zina, angafunike kupeleka uphungu wamphamvu. (1 Akor. 5:1-5) Ndipo akaona kuti ndise omvela komanso ogonjela, amakondwela kwambili.—Aheb. 13:17.

  • Abale na alongo akuyamikila woyang’anila dela na mkazi wake

    Onetsani kuyamikila. Uzani woyang’anila dela na mkazi wake mmene mumapindulila cifukwa ca khama lawo. Mungacite zimenezi mwa kuwauza mwacindunji kapena mwa kuwapatsa khadi olo kuwalembela kakalata.—Akol. 3:15.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani