LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w24 December tsa. 32
  • Anthu Okhulupilika Amasunga Malonjezo Awo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Anthu Okhulupilika Amasunga Malonjezo Awo
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2024
  • Nkhani Zofanana
  • ‘Muzikwanilitsa Zimene Mwalonjeza’
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2017
  • Mulungu Amakonda Anthu Okhulupilika
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2016
  • Anakondweletsa Atate Wake ndi Yehova
    Phunzitsani Ana Anu
  • Yefita Anali Munthu Wauzimu
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2024
w24 December tsa. 32

ZIMENE MUNGACITE PA KUŴELENGA KWANU

Anthu Okhulupilika Amasunga Malonjezo Awo

Ŵelengani Oweruza 11:30-40 kuti muphunzile ku cocitika ca Yefita na mwana wake wamkazi pa nkhani yosunga malonjezo.

Mvetsani nkhani yonse. Kodi Aisiraeli okhulupilika anali kuwaona bwanji malonjezo awo kwa Yehova? (Num. 30:2) Kodi Yefita na mwana wake wamkazi, anaonetsa bwanji kuti anali na cikhulupililo mwa Yehova?​—Ower. 11:9-11, 19-24, 36.

Kumbani mozamilapo. Kodi Yefita analonjeza ciyani kwa Yehova? Nanga anatanthauza ciyani pamene anapanga lonjezolo? (w16.04 7 ¶12) Ni zinthu ziti zimene Yefita na mwana wake anadzimana kuti akwanilitse lonjezo lake? (w16.04 7-8 ¶14-16) Kodi ni malonjezo otani amene Akhristu angapange masiku ano?​—w17.04 5-8 ¶10-19.

Onani zimene muphunzilapo. Dzifunseni kuti:

  • ‘N’ciyani cinganithandize kusunga lonjezo langa la kudzipatulila?’ (w20.03 13 ¶20)

  • ‘Kodi ningadzimane zinthu ziti kuti nicite zambili potumikila Yehova?’

  • ‘N’ciyani cinganithandize kusunga lonjezo langa lokhalabe wokhulupilika kwa mnzanga wa mu ukwati?’ (Mat. 19:5, 6; Aef. 5:28-33)

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani