Mawu Amunsi
d Kuonongedwa kwa Babulo n’citsanzo cimodzi cabe ca maulosi a m’Baibo amene anakwanilitsika kale. Zitsanzo zina ndi za kuonongedwa kwa mzinda wa Turo ndi wa Nineve. (Ezekieli 26:1-5; Zefaniya 2:13-15) Ndiponso, ulosi wa Danieli unakambilatu za maulamulilo amphamvu a padziko amene anali kudzakhalapo motsatizana pambuyo pa ulamulilo wa Babulo. Maulamulilo amenewa anaphatikizapo maulamulilo a Amedi ndi Aperisiya, ndi wa Gilisi. (Danieli 8:5-7, 20-22) Onani Zakumapeto, pamapeji 199 mpaka 201, kuti mudziŵe maulosi ambili onena za Mesiya amene anakwanilitsika mwa Yesu Kristu.