b Yehova amachedwa kuti Atate cifukwa iye ndiye Mlengi. (Yesaya 64:8) Popeza kuti Yesu analengedwa ndi Mulungu, amachedwa Mwana wa Mulungu. Pa cifukwa cimodzi-modzi, zolengedwa zinanso zauzimu zimachedwa ana a Mulungu. Koma Adamu nayenso amachedwa mwana wa Mulungu.—Yobu 1:6; Luka 3:38.