Mawu Amunsi
a Apa sititanthauza kuti aliyense amene angakutsutseni ndiye kuti amatsogoleledwa ndi Satana mwacindunji. Koma Satana ndiye Mulungu wa dongosolo lino la zinthu, ndipo dziko lonse lili m’manja mwake. (2 Akorinto 4:4; 1 Yohane 5:19) Mwa ici, anthu ena sadzatikonda cifukwa cokhala ndi umoyo wokondweletsa Mulungu, ndipo ena adzatitsutsa.