Mawu Amunsi
a Kucokela mu October caka ca 607 B.C.E. kufika mu October caka ca 1 B.C.E. panapita zaka 606. Kucokela mu October caka ca 1 B.C.E. mpaka mu October 1914 C.E. panapita zaka 1,914. Tikaonkhetsa zaka 606 ndi 1,914, tipeza zaka 2,520. Kuti mudziŵe zambili zokhudza kuonongedwa kwa Yerusalemu mu caka ca 607 B.C.E., onani buku lakuti Kukambitsirana za m’Malemba, pamapeji 231 mpaka 233, lolembedwa ndi Mboni za Yehova.