Mawu Amunsi
b Baibulo limaonetsa kuti, kungokhala ndi cikumbumtima coyela sikokwanila. Mwacitsanzo, mtumwi Paulo anati: “Sindikudziŵa kanthu kalikonse konditsutsa mumtima mwanga. Koma zimenezi sizikutanthauza kuti basi ndine wolungama, koma Yehova ndiye amandifufuza.” (1 Akorinto 4:4) Ngakhale anthu amene amazunza Akristu, monga mmene Paulo anali kucitila, angacite zimenezo ndi cikumbumtima coyela, ndi kumaganiza kuti Mulungu amavomeleza zocita zao. Conco, n’kofunika kuti cikumbumtima cathu cikhale coyela kwa ife ndi kwa Mulungu.—Machitidwe 23:1; 2 Timoteyo 1:3.