Mawu Amunsi
c Mulungu ni amene anabweletsa Cigumula cimeneci ndipo zikuoneka kuti cinafafanizilatu munda wa Edeni. Lemba la Ezekieli 31:18 limasonyeza kuti pofika zaka za m’ma 1600 B.C.E. “mitengo ya mu Edeni” inali itatha kale. Conco onse amene anayesetsa kufuna-funa malo amene panali munda wa Edeni anangotaya nthawi cifukwa sakanaupeza.