Mawu Amunsi
g Ponena za ulosi wokhudza masiku otsiliza Yesu anati: “Anthu amitundu ina adzapondaponda Yerusalemu [amene akuimila ulamulilo wa Mulungu], kufikila nthawi zoikidwilatu za anthu amitundu inawo zitakwanila.” (Luka 21:24) Conco tinganene kuti kusokonezedwa kwa ulamulilo wa Mulungu kunali kudakalipo pamene Yesu anali padziko lapansi ndipo kunayenela kupitilizabe mpaka m’masiku otsiliza.