Mawu Amunsi
a Tikamati “coonadi,” nthawi zambili timatanthauza zimene timakhulupilila komanso umoyo wathu wacikhristu. Kaya ndife atsopano m’coonadi kapena aciyambakale, tingapindule kwambili mwa kuganizila cimene cinatipangitsa kuyamba kukonda coonadi. Tikatelo, tidzakhala ofunitsitsa kucita zokondweletsa Yehova.