Mawu Amunsi
b Nthawi zina, akulu mu mpingo amaweluza nkhani zokhudza macimo aakulu komanso kulapa. (1 Akor. 5:11; 6:5; Yak. 5:14, 15) Komabe, modzicepetsa iwo amakumbukila kuti sangadziŵe za mu mtima mwa munthu, ndiponso kuti akuweluzila Yehova. (Yelekezelani na 2 Mbiri 19:6.) Iwo mosamala amapanga zigamulo motsatila cifundo ca Mulungu na mfundo zake zolungama.