Mawu Amunsi
a Nkhani ino, ifotokoza zinthu zitatu zimene Yehova amacita pothandiza alambili ake kupilila mavuto mwacimwemwe. Kuti tizidziŵe zinthu zimenezo, tikambilane mfundo za mu Yesaya caputala 30. Pokambilana caputala cimeneci, tidzakumbutsidwa kufunika kopemphela kwa Yehova, kuŵelenga Mawu ake, na kusinkhasinkha madalitso amene watipatsa, komanso amene watisungila m’tsogolo.