Mawu Amunsi
a Mtumwi Paulo analimbikitsa Akhristu anzake kusalola dongosolo lino la zinthu kuumba kaganizidwe kawo. Uwu ni uphungu wabwino ngakhale kwa ife masiku ano. Tiyenela kuyesetsa kusalola maganizo oipa a dzikoli kuumba kaganizidwe kathu mwa njila ina iliyonse. Kuti izi zitheke, tiyenela kupitiliza kuwongolela kaganizidwe kathu, nthawi zonse tikazindikila kuti sikogwilizana na cifunilo ca Mulungu. M’nkhani ino, tikambilane mmene tingacitile zimenezi.