Mawu Amunsi
a Yesu anakhalitsa bata cimphepo camphamvu, kucilitsa odwala, na kuukitsa akufa. N’zokondweletsa kwambili kuŵelenga zokhudza zozizwitsa zimene Yesu anacita! Zozizwitsazo zinalembedwa m’Baibo kuti zitiphunzitse osati kungotisangalatsa. M’nkhani ino, tikambilane zina mwa zozizwitsazo, kuti tilimbitse cikhulupililo cathu pa zimene tiphunzilapo zokhudza Yehova na Yesu. Ndipo pa zozizwitsazo, tidzazindikilanso makhalidwe aumulungu amene tiyenela kukhala nawo.