Mawu Amunsi
a Ngakhale kuti tingakumane na mavuto osayembekezela m’dzikoli, ndife otsimikiza kuti Yehova amathandiza alambili ake okhulupilika. Kodi Yehova anawathandiza bwanji atumiki ake akale? Nanga amatithandiza bwanji ife masiku ano? Kukambilana zitsanzo za m’Baibo komanso zamakono, kudzatipatsa cidalilo cakuti nafenso Yehova adzatithandiza tikam’dalila.