Mawu Amunsi
a Nkhani ino itithandiza mmene tingathamangile pa mpikisano wokalandila moyo. Pamene tikuthamanga, pali zofunikila kunyamula. Izi ziphatikizapo lonjezo limene tinapanga podzipatulila, maudindo a m’banja, komanso kuyankha mlandu pa zisankho zathu. Komabe, tiyenela kutaya zolemetsa zilizonse zimene zingacepetse liŵilo lathu. Kodi zolemelazo ziphatikizapo ciyani? Nkhani ino iyankha funso limeneli.