Mawu Amunsi
b Nkhani zakuti “Mfundo Zothandiza Mabanja” mungazipeze pa jw.org ku Chichewa. Mwacitsanzo, nkhani yakuti “Kodi Mungasonyezane Bwanji Ulemu?,” komanso yakuti “Kodi Mungasonyeze Bwanji Kuti Mumayamikila Zimene Mwamuna kapena Mkazi Wanu Amacita?” zingathandize okwatilana. Nkhani yakuti “Phunzitsani Ana Anu Kugwilitsa Nchito Foni Mosamala,” komanso yakuti “Zimene Mungacite Kuti Muzimasukilana Ndi Mwana Wanu,” zingathandize makolo. Ndipo acinyamata angapindule na nkhani yakuti “Kodi Mungatani Kuti Musamangotengela Zocita za Anzanu?,” komanso yakuti “Kodi Mungatani Ngati Mumasoŵa Woceza Naye?”