Mawu Amunsi
a Malinga n’kunena kwa Baibo, pali chimo limene silingakhululukidwe. Chimo limenelo si mtundu wina wake wa chimo. Koma anthu amene amacita chimo limenelo ni aja amene amasankha kucita zinthu zotsutsana na Mulungu nthawi zonse. Komabe, ni Yehova yekha na Yesu amene amadziŵa kuti chimo limene munthu wacita ni losakhululukidwa.—Maliko 3:29; Aheb. 10:26, 27.