Mawu Amunsi
a Mwacitsanzo, Mkhristu mnzathu angasankhe kusagwila nchito kuti apeze zomuthandiza paumoyo ngakhale kuti angakwanitse kucita zimenezo. Mwina angasankhenso kukhala pa cibwenzi na munthu wosakhulupilila, kapena angayambe kufalitsa nkhani zotsutsa ziphunzitso zathu kapena kufalitsa mijedo yovulaza. (1 Akor. 7:39; 2 Akor. 6:14; 2 Ates. 3:11, 12; 1 Tim. 5:13) Mkhristu amene amacita zimenezi ndiye kuti “akuyenda mosalongosoka.”