Mawu Amunsi
a Mmene mawu a Ciheberi anawagwilitsila nchito palembali aonetsa kuti uku ndiye kukhululuka kwenikweni. Amaonetsanso kuti ndi Yehova yekhayo amene angakhululuke macimo ndi mtima wonse. Mu Mabaibulo ambili mulibe mfundo yofunika imeneyi palembali, koma mu Baibulo la Dziko Latsopano ilimo. Izi zimapangitsa Baibulo limeneli kukhala lapadela m’njila imene anamasulila lemba la Salimo 130:4.