LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
Mabuku a m’Cinyanja (2000-2026)
Tulukani
Loŵani
LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Lelo

Cisanu, October 31

Atatewo amakukondani cifukwa munandikonda ndipo mwakhulupilila kuti ine ndinabwela monga nthumwi ya Mulungu.​—Yoh 16:27.

Yehova amafuna-funa mipata yoonetsa anthu kuti amawakonda, komanso kuti amakondwela nawo. Malemba amakamba nthawi ziŵili pomwe Iye anauza Yesu kuti ni Mwana wake wokondedwa, ndiponso kuti amakondwela naye. (Mat. 3:17; 17:5) Kodi mungakonde kumva Yehova akukuuzani kuti amakondwela nanu? Yehova sakamba nafe mwacindunji masiku ano, koma amatelo kupitila m’Mawu ake. Timamva mawu a Yehova otitsimikizila kuti amakondwela nafe tikaŵelenga mawu a Yesu opezeka m’Mauthenga Abwino. Yesu anatengela bwino kwambili makhalidwe a Atate wake. Cotelo, tikamaŵelenga mawu a Yesu oonetsa kuti anali kuwakonda otsatila ake opanda ungwilo koma okhulupilika, zimakhala ngati tikumumva Yehova akutiuza mawu amenewo. (Yoh. 15:9, 15) Kukumana na mavuto si umboni wakuti Mulungu analeka kukondwela nafe. M’malo mwake, kumatipatsa mwayi woonetsa kuzama kwa cikondi cathu pa Mulungu, komanso kukula kwa cidalilo cathu mwa iye.​—Yak. 1:12. w24.03 28 ¶10-11

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Ciŵelu, November 1

Mwacititsa kuti mʼkamwa mwa ana ndi mwa makanda mutuluke mawu otamanda.​—Mat. 21:16.

Ngati ndinu kholo, thandizani ana anu kukonzekela ndemanga malinga na msinkhu wawo. Nthawi zina, timakambilana nkhani zikulu-zikulu monga zokhudza mavuto a m’banja kapena ciyelo ca mpingo. Koma pamakhalabe ndime imodzi kapena ziŵili zimene ana angapelekepo ndemanga. Cina, fotokozelani ana anu kuti si nthawi zonse pomwe angapatsidwe mwayi woyankhapo akakweza dzanja. Kucita izi kudzawathandiza kuti asamakhumudwe mwayi woyankhapo ukapatsidwa kwa ena. (1 Tim. 6:18) Tonsefe tingakonzekele ndemanga zogwila mtima zimene zimalemekeza Yehova, na kulimbikitsa Akhristu anzathu. (Miy. 25:11) Ngakhale kuti nthawi zina tingafunike kufotokoza mwacidule zocitika pa umoyo wathu, tiyenela kupewa kukamba kwambili za ife eni. (Miy. 27:2; 2 Akor. 10:18) M’malo mwake, tiziika kwambili maganizo athu pa Yehova, Mawu ake, komanso anthu ake.​—Chiv. 4:11. w23.04 24-25 ¶17-18

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Sondo, November 2

Tisapitilize kugona ngati mmene ena onse akucitila, koma tikhalebe maso ndipo tikhalebe oganiza bwino.​—1 Ates. 5:6.

Cikondi n’cofunika kwambili kuti tikhalebe maso komanso oganiza bwino. (Mat. 22:37-39) Kukonda Mulungu kumatithandiza kupilila mavuto amene tingakumane nawo tikamalalikila. (2 Tim. 1:7, 8) Popeza timakondanso anthu amene satumikila Mulungu, timapitilizabe kulalikila pafoni na m’makalata. Timakhala na ciyembekezo cakuti tsiku lina, iwo adzasintha umoyo wawo na kuyamba kucita zabwino. (Ezek. 18:27, 28) Timakondanso Akhristu anzathu. Ndipo timaonetsana cikondi cimeneco mwa “kutonthozana ndi kulimbikitsana.” (1 Ates. 5:11) Monga asilikali amene amaseŵenzela pamodzi pa nkhondo, timalimbikitsana. Sitingakhumudwitse abale na alongo athu mwadala, kapena kubwezela coipa pa coipa. (1 Ates. 5:13, 15) Timaonetsanso cikondi cathu polemekeza abale amene akutsogolela mu mpingo.​—1 Ates. 5:12. w23.06 10 ¶6; 11 ¶10-11

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani