LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
Cilengezo
Taikaponso citundu cina: Shan
  • Lelo

Ciŵelu, September 6

Muzipeleka citsanzo cabwino kwa gulu la nkhosa.​—1 Pet. 5:3.

Upainiya umathandiza wacinyamata kuphunzila kuseŵenza bwino na anthu osiyana-siyana. Umam’thandizanso kupanga bajeti yabwino na kuitsatila. (Afil. 4:11-13) Ciyambi cabwino coyamba utumiki wa nthawi zonse ni kucita upainiya wothandiza umene umawathandiza kuti ayambe upainiya wa nthawi zonse. Upainiya wa nthawi zonse umatsegula mipata ku mautumiki ena a nthawi zonse osiyana-siyana, monga kutumikila m’dipatimenti ya zamamangidwe kapena pa Beteli. Amuna acikhristu ayenela kukhala na colinga cokwanilitsa ziyeneletso kuti atumikile abale na alongo awo mu mpingo monga akulu. Baibo imati amuna amene akuyesetsa kuti akhale oyang’anila “akufuna nchito yabwino.” (1 Tim. 3:1) Coyamba, m’bale afunika kuyenelela kukhala mtumiki wothandiza. Atumiki othandiza amathandiza akulu m’njila zosiyana-siyana. Akulu na atumiki othandiza amatumikila abale na alongo awo modzicepetsa ndipo amalalikila mokangalika. w23.12 28 ¶14-16.

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Sondo, September 7

Akadali mnyamata, . . . anayamba kufunafuna Mulungu wa Davide kholo lake.​—2 Mbiri 34:3.

Mfumu Yosiya anayamba kufuna-funa Yehova ali mnyamata. Anali wofunitsitsa kuphunzila za Yehova na kucita cifunilo cake. Komabe, umoyo sunali wopepuka kwa mfumu yacinyamatayi. Anafunika kulimba mtima kuti abwezeletse kulambila koyela panthawi imene kulambila konyenga kunali kofala. Ndipo anatelodi! Asanakwanitse zaka 20, Yosiya anayamba kucotsa kulambila konyenga m’dzikolo. (2 Mbiri 34:1, 2) Ngakhale kuti ndinu wacicepele kwambili, mungathe kutengela Yosiya mwa kufuna-funa Yehova na kuphunzila za makhalidwe ake. Izi zingakulimbikitseni kupatulila moyo wanu kwa iye. Kodi kudzipatulila kumeneku kudzakhudza bwanji umoyo wanu wa tsiku na tsiku? Pa tsiku limene anali kubatizika, ali na zaka 14, Luke anati, “Kuyambila lelo, nidzaika kutumikila Yehova patsogolo mu umoyo wanga, ndipo nidzayesetsa kumukondweletsa.” (Maliko 12:30) Ngati ni zimene nanunso mufuna kucita, mudzadalitsika kwambili! w23.09 11 ¶12-13

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Mande, September 8

Muzilemekeza anthu amene akugwila nchito mwakhama pakati panu, amenenso amakutsogolelani mwa Ambuye.​—1 Ates. 5:12.

Pamene mtumwi Paulo analemba kalatayi, mpingo wa Atesalonika unali usanakwanitse caka. N’kutheka kuti amuna apaudindo mumpingowo anali acatsopano, ndipo anali kulakwitsa zina. Ngakhale n’telo, anayenela kulemekezedwa. Pamene cisautso cacikulu cikuyandikila, tidzafunika kudalila kwambili citsogozo ca akulu kuposa kale lonse. Nthawi zina sizingatheke kulandila malangizo ocokela ku likulu lathu kapena ku ofesi ya nthambi. Conco, m’pofunika kwambili palipano kuphunzila kuwakonda akulu na kuwalemekeza. Kaya pacitike zotani, tiyeni tikhalebe oganiza bwino, na kupewa kuyang’ana zophophonya zawo. M’malo mwake, tiziika maganizo athu pa mfundo yakuti Yehova kudzela mwa Khristu, akutsogolela amuna okhulupilika amenewa. Monga mmene cisoti cimatetezela mutu wa msilikali, naconso ciyembekezo cathu cacipulumutso cimateteza maganizo athu. Timaona kuti zimene dzikoli limapeleka n’zopanda phindu. (Afil. 3:8) Cimatithandizanso kukhala odekha komanso osasunthika. w23.06 11-12 ¶11-12

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani