-
Sangalalani Cifukwa Cogwila Nchito Yanu Mwakhama“Khalanibe m’Cikondi ca Mulungu”
-
-
6, 7. Kodi Yesu ali ndi mbili yotani pa nkhani yogwila nchito mwakhama?
6 Yesu ali ndi mbili yabwino yogwila nchito mwakhama kwa nthawi yaitali. Asanabwele padziko lapansi, iye anatumikila monga “mmisili waluso” wa Mulungu polenga zinthu zonse “zakumwamba ndi zapadziko lapansi.” (Miyambo 8: 22-31; Akolose 1:15-17) Pamene anali padziko lapansi, Yesu anapitilizabe kugwila nchito mwakhama. Akali mwana, iye anaphunzila nchito yomanga ndipo anali kudziŵika kuti ndi “mmisili wamatabwa.”a (Maliko 6:3) Nchito imeneyi imafuna mphamvu ndi luso, makamaka panthawi imene kunalibe makina amakono ocekela matabwa, masitolo ogulako zofunikila ndi zipangizo zamagetsi. Yelekezani kuti mukuona Yesu akupita kukafunafuna mitengo, kuidula, kuigubuduza mpaka kumalo ake ogwilila nchito. Kenako mukumuona akumanga nyumba, kukhoma denga, kupanga zitseko ndi zinthu zina zamatabwa. N’zosacita kufunsa kuti Yesu anali kusangalala cifukwa cogwila nchito mwakhama ndi mwaluso.
-
-
Sangalalani Cifukwa Cogwila Nchito Yanu Mwakhama“Khalanibe m’Cikondi ca Mulungu”
-
-
a Buku lina linati, liu la Cigiriki lomasulidwa kuti “mmisili wamatabwa,” ndi “dzina la munthu amene amagwilitsila nchito matabwa pomanga nyumba kapena zinthu zina zilizonse za matabwa.”
-