-
Tanthauzo Lake la Kusakhalila MbaliKondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
-
-
PHUNZILO 45
Tanthauzo la Kusakhalila Mbali
Yesu anaphunzitsa otsatila ake kuti sayenela kukhala “mbali ya dzikoli.” (Yohane 15:19) Izi zikutanthauza kusakhalila mbali m’ndale za dziko kapena pankhondo. Kunena zoona, nthawi zina si cinthu capafupi kusakhalila mbali. Zili conco cifukwa anthu ena amatinyodola cifukwa ca kutelo. Koma kodi tingacite bwanji kuti tisamakhalile mbali, komano n’kukhala wokhulupilikabe kwa Yehova Mulungu?
1. Kodi Akhristu oona amaaona motani maboma a anthu?
Akhristu amalemekeza boma. Timacita zimene Yesu ananena kuti: “Pelekani zinthu za Kaisara kwa Kaisara.” Mwa ici, timamvela malamulo a boma monga a kukhoma misonkho. (Maliko 12:17) Baibo imatiuza kuti maboma a anthu alipo cabe cifukwa Yehova anawalola kulamulila. (Aroma 13:1) Conco, timadziŵa kuti maboma a anthu ali na ulamulilo inde, koma ulamulilo wawo ni wocepelapo. Ciyembekezo cathu maka-maka cagona mwa Mulungu amene adzacotsapo mavuto onse a anthu kupyolela mu Ufumu wake wakumwamba.
2. Kodi tingaonetse bwanji kuti sitimakhalila mbali?
Potengela citsanzo ca Yesu, ifenso sitiyenela kutengako mbali m’ndale za dziko. Anthu ataona kuti Yesu wacita cozizwitsa, anayesa kumulonga ufumu padziko lapansi, koma iye sanalole zimenezo. (Yohane 6:15) Cifukwa ciyani? Iye anakamba kuti, “Ufumu wanga suli mbali ya dziko lino.” (Yohane 18:36) Pokhala otsatila a Yesu, ifenso sitikhalila mbali m’njila iliyonse. Mwacitsanzo, sitipita ku nkhondo. (Ŵelengani Mika 4:3.) Inde, zizindikilo za maiko monga mbendela timazilemekeza. Ngakhale n’telo, sitizipangila saliyuti cifukwa n’cimodzi-modzi na kuzilambila. (1 Yohane 5:21) Ndipo tikabwela ku nkhani zandale, sitikhalila mbali cipani ciliconse, kapena aliyense woimilila pa masankho. Mwa njila zimenezi komanso zina, timaonetsa kuti ndife wokhulupilika kwathunthu ku boma la Mulungu—Ufumu wake.
KUMBANI MOZAMILAPO
Onani zocitika zimene zingatiike pa mayeso pankhani ya kusakhalila mbali na mmene mungapangile zisankho zokondweletsa Yehova.
3. Akhristu oona sakhalila mbali m’nkhani za dziko
Yesu Khristu pamodzi na otsatila ake anatisiila citsanzo cabwino kwambili. Ŵelengani Aroma 13:1, 5-7, komanso 1 Petulo 2:13, 14. Pambuyo pake, tambani VIDIYO na kukambilana mafunso otsatila.
N’cifukwa ciyani maboma a anthu tiyenela kuwalemekeza?
Ndipo tingaonetse kuwamvela m’njila ziti?
Pa nthawi ya nkhondo, maiko ena anganene kuti sakhalila mbali, koma kuseli amakhala akuthandizila maiko amene akumenyana. Kodi kusakhalila mbali kwazoona n’kotani? Ŵelengani Yohane 17:16. Pambuyo pake, tambani VIDIYO na kukambilana funso lotsatila.
Kodi kusakhalila mbali kumatanthauza ciyani?
Bwanji ngati olamulila a dziko atiuza kucita cinthu cina cosemphana na lamulo la Mulungu? Ŵelengani Machitidwe 5:28, 29. Pambuyo pake, tambani VIDIYO na kukambilana mafunso otsatila.
Pakakhala kuwombana pakati pa lamulo la anthu na lamulo la Mulungu, kodi tiyenela kumvela lamulo la ndani?
Kodi mungaganizileko zocitika zilizonse pamene Akhristu sayenela kumvela maboma a anthu?
4. Musamakhalile mbali m’maganizo komanso m’zocita
Ŵelengani 1 Yohane 5:21. Pambuyo pake, tambani VIDIYO na kukambilana mafunso otsatila.
Mu vidiyo imeneyi, n’cifukwa ciyani Ayenge sanaloŵeko cipani ca ndale, kapena kucitako mwambo wokweza dziko lake, monga kucitako mwambo wotamanda mbendela?
Kodi muganiza kuti iye anapanga cisankho canzelu?
Ni zocitika zina ziti zingakuikeni pa mayeso pankhani ya kusakhalila mbali? Tambani VIDIYO, kenako kambilanani mafunso otsatila.
Kodi tingapewe bwanji kukhalila mbali pamene maiko akupikisana pa zocitika za maseŵelo?
Kodi tingapewe bwanji kukhalila mbali pamene anthu andale apanga zigamulo zimene ifenso zimatikhudza?
Tikapanda kusamala, kodi tingayambe bwanji kukhalila mbali cifukwa ca nkhani za panyuzi kapena anthu amene timaceza nawo?
Kodi Mkhristu ayenela kupewa kukhalila mbali pa nkhani ziti m’maganizo komanso m’zocita zake?
MUNTHU WINA ANGAFUNSE KUTI: “N’cifukwa ciyani simucitako mwambo wotamanda mbendela kapena kuimbako nyimbo ya fuko?”
Kodi inu mungayankhe bwanji?
CIDULE CAKE
Akhristu amayesetsa kusakhalila mbali pankhani zandale m’maganizo mwawo, m’zokamba zawo, ngakhalenso m’zocita zawo.
Mafunso Obweleza
Kodi tiyenela kucita motani ku maboma a anthu?
N’cifukwa ciyani tiyenela kupewelatu kukhalila mbali m’nkhani zandale?
Kodi n’zocitika ziti zingatiike pamayeso pa nkhani ya kusakhalila mbali?
FUFUZANI
Kodi tingafunike kudzimana zinthu zotani kuti tipewe kukhalila mbali?
Kodi mabanja angakonzekele bwanji mayeso pankhani ya kusakhalila mbali?
Kusatenga Mbali M’zandale pa Miyambo na Zikondwelelo za Dziko (4:25)
N’cifukwa ciyani kuteteza dziko lanu sindiwo ulemu wopambana umene munthu angalandile?
Pa nkhani yosankha nchito, ganizilani mmene mungapewele kukhala mbali ya dziko.
“Yense Adzasenza Katundu Wake wa Iye Mwini” (Nsanja ya Olonda, March 15, 2006)
-
-
Mukhoza Kupilila Pamene MukuzunzidwaKondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
-
-
Pa nthawi inayake, Akhristu tonse tidzakumana na anthu otitsutsa ngakhale kutizunza. Kodi zimenezi ziyenela kutidetsa nkhawa?
1. N’cifukwa ciyani tiyenela kuyembekezela mazunzo?
Baibo imakamba momveka bwino kuti: “Onse ofuna kukhala ndi moyo wodzipeleka kwa Mulungu mwa Khristu Yesu, nawonso adzazunzidwa.” (2 Timoteyo 3:12) Yesu anazunzidwa cifukwa sanali kumbali ya dziko la Satanali. Ifenso sitili kumbali ya dzikoli. Conco, sitikudabwa pamene maboma kapena zipembedzo za dzikoli zikutizunza.—Yohane 15:18, 19.
2. Kodi mazunzo tingawakonzekele bwanji?
Tiyenela kulimbitsa cikhulupililo cathu mwa Yehova pali pano. Tsiku lililonse, tiyenela kupemphela kwa Yehova na kuŵelenga Mawu ake. Tiyenelanso kupezeka ku misonkhano nthawi zonse. Izi n’zimene muyenela kucita kuti mukhale na mphamvu, komanso wolimba mtima kupilila cizunzo ciliconse, ngakhale citacokela kwa a m’banja mwanu. Mtumwi Paulo, amenenso anakumana na mazunzo kaŵili-kaŵili, analemba kuti: “Yehova ndiye mthandizi wanga. Sindidzaopa.”—Aheberi 13:6.
Timakhalanso olimba mtima tikamalalikila nthawi zonse. Kulalikila kumatiphunzitsa kudalila Yehova na kusaopa munthu aliyense. (Miyambo 29:25) Mukazoloŵela kulalikila molimba mtima pali pano, simungaleke kulalikila ngakhale boma litaletsa nchito yathu imeneyi.—1 Atesalonika 2:2.
3. Kodi pali ubwino wanji tikapilila cizunzo?
Pamene tikuzunzidwa sikuti timasangalala ayi. Koma tikakwanitsa kupilila, cikhulupililo cathu cimakhala colimba. Ndipo cikondi cathu pa Yehova cimakula, cifukwa timaona mmene amatithandizila pamene sitingathenso kupilila. (Ŵelengani Yakobo 1:2-4.) Pamene anthu ena akutivutitsa, Yehova cimamuŵaŵa kwambili. Koma mtima wake umakondwela akaona kuti tikupilila. Baibo imakamba kuti: “Ngati mukupilila povutika cifukwa ca kucita zabwino, zimenezo n’zabwino kwa Mulungu.” (1 Petulo 2:20) Anthu onse amene amapilila mokhulupilika, Yehova adzawapatsa mphoto. Mphoto imeneyo ni moyo wosatha m’dziko lopanda anthu otsutsa kulambila koona—Mateyu 24:13.
KUMBANI MOZAMILAPO
Onani cifukwa cake n’kotheka komanso n’kopindulitsa kukhalabe wokhulupilika kwa Yehova, ngakhale pamene tikuzunzidwa.
4. Mukhoza kupilila ngati a m’banja mwanu akukutsutsani
Yesu anakambilatu mfundo yakuti zikhoza kucitika a m’banja mwathu kusagwilizana na cisankho cathu colambila Yehova. Ŵelengani Mateyu 10:34-36, na kukambilana funso ili:
Kodi cingacitike n’ciyani ngati wina m’banja wasankha kutumikila Yehova?
Kuti muone citsanzo ca zimenezi, tambani VIDIYO, kenako kambilanani funso lotsatila.
Kodi mungacite bwanji ngati wacibale wanu, kapena mnzanu, akuyesa kukuletsani kutumikila Yehova?
Ŵelengani Salimo 27:10, komanso Maliko 10:29, 30. Pambuyo poŵelenga lililonse la malembawa, kambilanani funso ili:
Kodi lonjezo limeneli lingakuthandizeni bwanji ngati a m’banja mwanu, kapena mabwenzi anu, akukuletsani kutumikila Yehova?
5. Pitilizani kulambila Yehova pamene mukuzunzidwa
Pamafunika kulimba mtima kuti titumikile Yehova pamene ena akutiletsa kutelo. Tambani VIDIYO, kenako kambilanani funso lotsatila.
Mu zitsanzo za mu vidiyo imeneyi, kodi cakulimbikitsani n’ciyani?
Ŵelengani Machitidwe 5:27-29, komanso Aheberi 10:24, 25. Pambuyo poŵelenga lililonse la malembawa, kambilanani funso ili:
N’cifukwa ciyani sitiyenela kuleka kulambila Yehova, ngakhale pamene boma laletsa nchito yathu yolalikila, kapena kusonkhana kwathu?
6. Yehova adzakuthandizani kuti mupilile
A Mboni za Yehova osiyana-siyana misinkhu na zikhalidwe, akhala akumutumikilibe Yehova mokhulupilika ngakhale pokumana na mazunzo. Kuti muone zimene zawathandiza, tambani VIDIYO. Pambuyo pake kambilanani funso lotsatila.
Mu vidiyo iyi, kodi n’ciyani cinathandiza Mboni zimenezi kupilila?
Ŵelengani Aroma 8:35, 37-39, komanso Afilipi 4:13. Pambuyo poŵelenga lililonse la malembawa, kambilanani funso ili:
Kodi lemba limeneli likukutsimikizilani bwanji kuti mukhoza kupilila mayeso alionse?
Ŵelengani Mateyu 5:10-12, na kukambilana funso ili:
N’cifukwa ciyani mungakhalebe acimwemwe ngakhale pamene mukuzunzidwa?
Mamiliyoni a olambila Yehova apilila mosagonja kwa owatsutsa. Inunso mukhoza kutelo!
ANTHU ENA AMAKAMBA KUTI: “Ine siningakwanitse kupilila cizunzo.”
Kodi ni malemba ati angawapatse cidalilo?
CIDULE CAKE
Yehova amayamikila tikamacitabe khama kumutumikila pamene tikuzunzidwa. Mwa thandizo lake, tidzakwanitsa kupilila!
Mafunso Obweleza
N’cifukwa ciyani Akhristu ayenela kuyembekezela kuti adzazunzidwa?
Kodi muyenela kucita ciyani pali pano kuti mukakhale wokonzeka pamene cizunzo cidzafika?
Kodi n’ciyani cingakupatseni cidalilo cakuti mudzamutumikilabe Yehova ngakhale pokumana na mayeso alionse?
FUFUZANI
Onani mmene m’bale wacicepele akufotokozela mmene Yehova anamuthandizila kupilila atamangidwa cifukwa cosakhalila mbali m’nkhani za dziko.
Onani cimene cinathandiza okwatilana aŵili kutumikila Yehova mokhulupilika kwa zaka zambili, mosasamala kanthu za kutsutsidwa.
Anatumikira Yehova Panthawi Imene Zinthu Zinali Zitasintha (7:11)
Onani mmene mungakhalile olimba mtima pamene mukuzunzidwa.
“Konzekelani Cizunzo Pali Pano” (Nsanja ya Mlonda, July 2019)
Kodi tiyenela kukumbukila ciyani a m’banja mwathu akamatitsutsa, ndipo tingathane nawo bwanji mavuto amene amakhalapo?
“Coonadi ‘Sicibweletsa Mtendele Koma Lupanga’” (Nsanja ya Mlonda, October 2017)
-