-
Kudyetsa Anthu Ambili Mwa Kugwilitsila Nchito Anthu OcepaNsanja ya Mlonda—2013 | July 1
-
-
8. Pa Pentekosite, kodi okhulupilila atsopano anaonetsa bwanji kuti anali kudziŵa bwino njila imene Kristu anali kugwilitsila nchito?
8 Kuyambila pa Pentekosite mu 33 C.E., Kristu amene anali ataukitsidwa, anagwilitsila nchito atumwi monga njila yogaŵila cakudya ca kuuzimu kwa ophunzila ena odzozedwa. (Ŵelengani Machitidwe 2:41, 42.) Njila imeneyo inali yodziŵika bwino kwa Ayuda ndi kwa anthu oloŵa Ciyuda amene anakhala Akristu odzozedwa ndi mzimu patsikulo. Mosazengeleza, io “anapitiliza kulabadila zimene atumwiwo anali kuphunzitsa.” Malinga ndi katswili wina, liu la Cigiriki limene analitembenuza kuti “anapitiliza kulabadila,” lingatanthauze kukhala “okhulupilika nthawi zonse ndi wa maganizo osumika pa cinthu cimodzi pocita zinthu.” Okhulupilila atsopano amenewo anali ndi njala yaikulu ya cakudya ca kuuzimu, ndipo anali kudziŵa bwino kumene angacipeze. Mokhulupilika, io anali kudalila atumwi kuti awafotokozele tanthauzo la mau ndi zocita za Yesu. Anali kuwadalilanso kuti awathandize kumvetsetsa mfundo zina za m’malemba zimene zimanena za iye.c—Mac. 2:22-36.
-
-
Kudyetsa Anthu Ambili Mwa Kugwilitsila Nchito Anthu OcepaNsanja ya Mlonda—2013 | July 1
-
-
c Ndime 8: Mfundo yakuti okhulupilila atsopano “anapitiliza kulabadila zimene atumwiwo anali kuphunzitsa,” imatanthauza kuti atumwi anali kuphunzitsa nthawi zonse. Zinthu zina zimene atumwi anali kuphunzitsa zinalembedwa m’mabuku ouzilidwa amene pa nthawi ino ndi mbali ya Malemba Acigiriki Acikristu.
-