LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • Kodi Baibo Imati Ciyani pa Nkhani ya Umbeta na Ukwati?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
    • 5. Sankhani mwanzelu munthu wokwatilana naye

      Kusankha munthu womanga naye banja ni nkhani yaikulu kwambili. Ŵelengani Mateyu 19:4-6, 9, na kukambilana funso ili:

      • N’cifukwa ciyani Mkhristu sayenela kuthamangila kuloŵa m’banja?

      Baibo ingakuthandizeni kudziŵa makhalidwe abwino a munthu amene mungakwatilane naye. Koma cofunika kwambili ni kupeza munthu amene amakonda Yehova.b Ŵelengani 1 Akorinto 7:39 na 2 Akorinto 6:14. Ndiyeno kambilanani mafunso aya:

      • N’cifukwa ciyani tiyenela kukwatilana na Mkhristu mnzathu cabe?

      • Kodi muganiza kuti Yehova angamve bwanji tikakwatilana na munthu amene sakonda Mulungu?

      Nkhunzi yamphamvu na bulu wamng’ono, zonse zikuvutika m’joko.

      Mukamanga mujoko nyama ziŵili zosiyana kwambili, zonse zidzavutika. Mofananamo Mkhristu akamanga ukwati na munthu wosakhulupilila, adzakhala na mavuto ambili

  • Kodi Baibo Imati Ciyani pa Nkhani ya Umbeta na Ukwati?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
Mabuku a m’Cinyanja (2000-2026)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani