-
Utumiki Wopeleka Thandizo Pakacitika NgoziUfumu wa Mulungu Ukulamulila
-
-
6. (a) Malinga ndi mau a Paulo, n’cifukwa ciani nchito yopeleka thandizo ndi mbali ya kulambila kwathu? (b) Fotokozani mmene nchito yathu yopeleka thandizo imacitikila padziko lonse masiku ano. (Onani chati cakuti “Pakacitika Ngozi,” patsamba 214.)
6 Paulo anathandiza Akristu a ku Korinto kuzindikila kuti nchito yopeleka thandizo ndi mbali ya kulambila Yehova, ndiponso kuti ndi mbali ya utumiki wao kwa Iye. Onani kuti iye anakamba kuti Akristu amene amapeleka thandizo amacita zimenezo cifukwa ‘cogonjela uthenga wabwino wonena za Kristu.” (2 Akor. 9:13) Conco, cimene cimalimbikitsa Akristu kuthandiza anzao ndi mtima wao wofuna kutsatila zimene Kristu anaphunzitsa. Paulo ananena kuti zinthu zabwino zimene Akristu amacitila abale ao zimaonetsa “kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu.” (2 Akor. 9:14; 1 Pet. 4:10) Conco, ponena za nchito yothandiza abale athu amene akuvutika, magazini ya Nsanja ya Olonda ya December 1, 1975 inati: “Tisakaikile kuti Yehova Mulungu ndi Mwana wake Yesu Kristu amaona utumikiwu kukhala wofunika kwambili.” Zoonadi, nchito yopeleka thandizo ndi mbali yofunika kwambili ya utumiki wopatulika.—Aroma 12:1, 7; 2 Akor. 8:7; Aheb. 13:16.
-
-
Utumiki Wopeleka Thandizo Pakacitika NgoziUfumu wa Mulungu Ukulamulila
-
-
7, 8. Kodi colinga coyamba ca utumiki wathu wopeleka thandizo n’ciani? Fotokozani.
7 Kodi colinga ca utumiki wathu wopeleka thandizo pa nthawi yamavuto n’ciani? Paulo anayankha funso limenelo m’kalata yake yaciŵili yopita kwa Akorinto. (Ŵelengani 2 Akorinto 9:11-15.) Palembali, Paulo anafotokoza zolinga zitatu zimene timakwanilitsa tikamacita “utumiki wothandiza anthu” panthawi ya mavuto. Tiyeni tikambilane zolinga zimenezi.
8 Coyamba, utumiki umenewu umalemekeza Yehova. Onani kuti pa mavesi asanu a pa 2 Akorinto 9:11-15, Paulo anagwilitsila nchito mau angapo othandiza abale kuona mmene utumiki wopeleka thandizo umakhudzila Yehova Mulungu. Iye anawakumbutsa kuti utumikiwu umacititsa “anthu kuyamika Mulunguyo” ndiponso “kupeleka mapemphelo oculuka oyamika Mulungu.” (vesi 11 ndi 12) Anafotokozanso kuti nchito yopeleka thandizo imalimbikitsa Akristu ‘kulemekeza Mulungu’ ndi kuyamikila ‘kukoma mtima kwakukulu kwa Mulungu.’ (vesi 13 ndi 14) Ndiyeno Paulo anamaliza nkhani yake yonena za kupeleka thandizo ndi mau akuti: “Tikuyamika Mulungu.”—Vesi 15; 1 Pet. 4:11.
9. Kodi nchito yopeleka thandizo ingathandize anthu kukhala ndi maganizo otani? Pelekani citsanzo.
9 Mofanana ndi Paulo, atumiki a Mulungu lelolino amaona nchito yopeleka thandizo kukhala mwai wao wolemekeza Yehova ndi kukometsela ciphunzitso cake. (1 Akor. 10:31; Tito 2:10) Ndipo nchitoyi imathandiza kwambili kucotsa maganizo olakwika amene anthu ena ali nao ponena za Yehova ndi Mboni zake. Mwacitsanzo, m’dela lina limene linakhudzidwa ndi cimphepo camkuntho, munali kukhala mai wina amene anali ataika cikwangwani pa citseko ca nyumba yake colembedwa kuti: “Pano Sitifuna a Mboni za Yehova.” Tsiku lina, maiyo anaona anthu opeleka thandizo pakacitika ngozi zacilengedwe akukonza nyumba ina pafupi ndi nyumba yake. Kwa masiku angapo, iye anali kuona anthuwo akugwila nchito limodzi mogwilizana. Kenako anapita pamalowo kukafunsa kuti anthuwo anali ndani. Atadziŵa kuti anali a Mboni za Yehova, anacita cidwi kwambili ndipo anati: “Sindinali kudziŵa kuti anthu inu ndinu otele.” Kodi maiyo anacita ciani pambuyo pake? Anacotsa cikwangwani cija pa citseko ca nyumba yake.
-