LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • Zimene Mungacite Kuti Muzipindula Kwambili Poŵelenga Baibo
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
    • 3. Kodi mungapatule bwanji nthawi yoŵelenga Baibo?

      Kodi cimakuvutani kupeza nthawi yoŵelenga Baibo? Ambili cimativuta. Muziyesetsa ‘kugwilitsa nchito bwino nthawi yanu.’ (Aefeso 5:16) Mungacite zimenezi mwa kukhazikitsa nthawi yoŵelenga Baibo tsiku na tsiku. Anthu ena amapatula nthawi yoŵelenga Baibo m’mamaŵa tsiku lililonse. Ena amasankha nthawi ina monga popuma masana. Ndiponso ena amaŵelenga Baibo usiku asanagone. Nanga inu, ni nthawi iti ingakukomeleni?

  • Mmene Tingapangile Zisankho Zabwino
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
    • 3. Lolani kuti Baibo ikutsogoleleni

      Kodi mfundo za m’Baibo zingatitsogolele motani popanga zisankho? Tambani VIDIYO, kenako kambilanani mafunso otsatila.

      VIDIYO: Lolani Mfundo za m’Baibo Kukutsogolelani (5:54)

      • Kodi ufulu wodzisankhila zocita n’ciyani?

      • Nanga n’cifukwa ciyani Yehova anatipatsa ufulu wodzisankhila zocita?

      • Kodi iye anatipatsa ciyani cotithandiza kugwilitsa nchito bwino ufulu wodzisankhila zocita?

      Kuti muone citsanzo ca mfundo za m’Baibo, ŵelengani Aefeso 5:15, 16. Ndiyeno kambilanani mmene mungagwilitse “nchito bwino nthawi yanu” kuti . . .

      • muziŵelenga Baibo nthawi zonse.

      • mukhale mnzake wa mu ukwati wabwino, kholo labwino, kapena mwana womvela.

      • muzipezeka pa misonkhano ya mpingo.

  • Sankhani Zosangalatsa Zovomelezeka kwa Yehova
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
    • 2. N’cifukwa ciyani tiyenela kusamala nayo nthawi imene timathela pa zosangalatsa?

      Ngakhale titasankha zosangalatsa zabwino, tiyenelabe kusamala kuti zisatidyele nthawi yoculuka kwambili. Tikapanda kusamala tidzasoŵa nthawi yocita zinthu zofunika kwambili. Baibo imatilimbikitsa ‘kugwilitsa nchito bwino nthawi yathu.’—Ŵelengani Aefeso 5:15, 16.

  • Sankhani Zosangalatsa Zovomelezeka kwa Yehova
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
    • 4. Gwilitsani nchito nthawi yanu mwanzelu

      Tambani VIDIYO, kenako kambilanani funso lotsatila.

      VIDIYO: N’ciani Cimakulandani Nthawi? (2:45)

      • Ngakhale kuti m’bale wa mu vidiyo iyi sanali kutamba ciliconse coipa, kodi cinayamba kucitika kwa iye n’ciyani cifukwa cosasamala nayo nthawi yopumula?

      Ŵelengani Afilipi 1:10, na kukambilana funso ili:

      • Kodi lembali lingatithandize bwanji kusamala nayo nthawi yocita zosangulutsa?

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani