LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • N’ciyani Cingakuthandizeni Kuti Musaleke Kuphunzila Baibo?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
    • 4. Ikani kuphunzila Baibo patsogolo

      Nthawi zina tingakhale otangwanika kwambili na kuona kuti sitingapeze nthawi yophunzila Baibo. Kodi n’ciyani cingatithandize? Ŵelengani Afilipi 1:10, na kukambilana mafunso aya:

      • Kodi muganiza kuti zina mwa “zinthu zofunika kwambili” pa umoyo ni ziti?

      • Kodi mungacite bwanji kuti muike kuphunzila Baibo patsogolo?

      A. Zithunzi zoonetsa kuika miyala na mcenga m’bekete. 1. Mulu wa mcenga komanso mulu wa miyala ikulu-ikulu. 2. Bekete yothilamo mcenga wambili. 3. Miyalayo yakhala pamwamba pa mcenga ndipo ina yatsalako. B. Zithunzi: 1. Miyulu imodzimodziyo, wa mcenga komanso wa miyala. 2. Bekete imodzimodziyo koma yodzala na miyala. 3. Mcenga uloŵelela m’miyalayo, na kudzaza beketeyo mpaka pakamwa. Pangotsala tumcenga tocepa tumene situnaloŵe m’beketemo.
      1. Mukathila mcenga m’bekete, kenako n’kuikamo miyala, miyalayo siikwanamo ayi

      2. Koma mukayambilila kuikamo miyala, mudzakhala malo othilamo mcenga wambili. Mofananamo, ngati mutsogoza “zinthu zofunika kwambili” pa umoyo wanu, mudzakwanitsa kuzicita na kutsalako na nthawi yocitabe zinthu zina

      Tikamaphunzila Baibo timapeza zosowa zathu zauzimu—kutanthauza kuphunzila za Mulungu na kumulambila. Ŵelengani Mateyu 5:3, na kukambilana funso ili:

      • Kodi tikaika patsogolo kuphunzila Baibo, timapindula bwanji?

  • Sankhani Zosangalatsa Zovomelezeka kwa Yehova
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
    • 4. Gwilitsani nchito nthawi yanu mwanzelu

      Tambani VIDIYO, kenako kambilanani funso lotsatila.

      VIDIYO: N’ciani Cimakulandani Nthawi? (2:45)

      • Ngakhale kuti m’bale wa mu vidiyo iyi sanali kutamba ciliconse coipa, kodi cinayamba kucitika kwa iye n’ciyani cifukwa cosasamala nayo nthawi yopumula?

      Ŵelengani Afilipi 1:10, na kukambilana funso ili:

      • Kodi lembali lingatithandize bwanji kusamala nayo nthawi yocita zosangulutsa?

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani