-
Kodi Ena Mungawauzeko Bwanji Uthenga Wabwino?Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
-
-
1. Kodi anthu amene mumadziŵana nawo mungawauzeko bwanji zimene mukuphunzila?
Ophunzila a Yesu anakamba kuti: “Sitingaleke kulankhula zinthu zimene tinaziona ndi kuzimva.” (Machitidwe 4:20) Mfundo za coonadi zimene iwo anamva kwa Yesu anazikonda ngako, cakuti anali ofunitsitsa kuuzako munthu aliyense. Kodi inunso mumamva conco? Ngati n’telo, yesani kupeza mipata kuti mwaulemu, muziuzako acibale anu na mabwenzi anu zimene mukuphunzila.—Ŵelengani Akolose 4:6.
Njila zimene mungayambilepo
Pamene muceza na acibale anu, yambitsani nkhani ya m’Baibo ponena kuti: “Wiki ino naphunzila Mfundo yabwino kwambili.”
Ngati mnzanu akudwala kapena ali na nkhawa, muŵelengelenkoni lemba.
Anzanu a kunchito akakufunsani kuti kodi wikendi inali bwanji, auzenkoni zimene munaphunzila pa phunzilo lanu la Baibo, kapena pa msonkhano wa mpingo.
Onetsani mabwenzi anu webusaiti ya jw.org.
Muzipemphako anthu ena kukhalapo pa phunzilo lanu la Baibo, kapena aonetseni mmene angapemphele pa jw.org kuti wina aziphunzila nawo Baibo.
-
-
Kodi Ena Mungawauzeko Bwanji Uthenga Wabwino?Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
-
-
4. Khalani aulemu
Pouzako ena uthenga wabwino, musamangoganizila zimene mufuna kukamba, muziganilanso mozikambila. Ŵelengani 2 Timoteyo 2:24, komanso 1 Petulo 3:15, na kukambilana mafunso aya:
Kodi mungaseŵenzetse bwanji mfundo zili pa mavesi aya pouzako ena za m’Baibo?
Ngati acibale anu ena kapena anzanu sakuvomeleza zimene mukukamba, kodi muyenela kucita ciyani? Ndipo muyenela kupewa kucita ciyani?
N’cifukwa ciyani ni bwino kukambilana nawo mwaulemu, m’malo mowaumiliza kuti akhulupilile zimene mukukamba?
-