-
Oyang’anila Oweta Nkhosa za MulunguGulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
-
-
5 Mtumwi Paulo anandandalika ziyenelezo za m’Malemba zofunikila kwa oyang’anila, m’kalata yake yoyamba kwa Timoteyo, komanso ina yopita kwa Tito. Pa 1 Timoteyo 3:1-7 pamati: “Ngati munthu aliyense akuyesetsa kuti akhale woyang’anila, akufuna nchito yabwino. Conco woyang’anila akhale wopanda cifukwa comunenezela, mwamuna wa mkazi mmodzi, wosacita zinthu mopitilila malile, woganiza bwino, wadongosolo, woceleza alendo, ndiponso wotha kuphunzitsa. Asakhale munthu womwa moŵa mwaucidakwa, kapena wandewu, koma wololela. Asakhale waukali, kapena wokonda ndalama. Akhale mwamuna woyang’anila bwino banja lake. Wa ana omumvela ndi mtima wonse. (Ndithudi, ngati munthu sadziŵa kuyang’anila banja lake, ndiye mpingo wa Mulungu angausamalile bwanji?) Asakhale wotembenuka kumene, kuopela kuti angakhale wotukumuka cifukwa ca kunyada, n’kulandila ciweluzo cofanana ndi cimene Mdyelekezi analandila. Komanso, akhale woti ngakhale anthu akunja akumucitila umboni wabwino, kuti asatonzedwe ndi kukodwa mu msampha wa Mdyelekezi.”
-
-
Oyang’anila Oweta Nkhosa za MulunguGulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
-
-
7 Olo kuti poyamba ziyenelezo za m’Malemba zimenezi zingaoneke monga zovuta kuzifikila, amuna acikhristu sayenela kudodoma pokalamila udindo. Ngati alimbikila kukhala na makhalidwe acikhristu ofunikila kwa oyang’anila, amalimbikitsanso ena mumpingo kukalamila maudindo. Paulo analemba kuti colinga cotipatsila amunawo amene ni “mphatso,” n’cakuti “awongolele oyelawo, acite nchito yotumikila, amange thupi la Khristu, kufikila tonse tidzafike pa umodzi m’cikhulupililo komanso pa kumudziŵa molondola Mwana wa Mulungu, inde, kufikila tidzakhale munthu wacikulile, wofika pa msinkhu waucikulile umene Khristu anafikapo.”—Aef. 4:8, 12, 13.
-