-
Oyang’anila Oweta Nkhosa za MulunguGulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
-
-
9 Oyenelela kukhala oyang’anila, ni aja amene amacita zinthu mwanzelu pa umoyo wawo. Ngati woyang’anila ni wokwatila, ayenela kukhala mwamuna wa mkazi mmodzi, komanso woyang’anila bwino banja lake. Ngati woyang’anila ali na ana okhulupilila amene amamumvela na mtima wonse, ndipo sanenezedwa kuti ni amakhalidwe oipa kapena osalamulilika, abale akhoza kumufikila mwacidalilo kufunsilako malangizo kapena nzelu pa nkhani zokhudza banja kapena umoyo wacikhristu. Ayenelanso kukhala wopanda cifukwa comuneneza naco, ndipo akhale munthu wakuti, ngakhale anthu akunja akumucitila umboni wabwino. Akhale woti sanganenezedwe za khalidwe loipa, zimene zingatonzetse mpingo. Asakhale woti anadzudzulidwa posacedwa cifukwa ca colakwa cacikulu. Ayenela kukhala citsanzo cimene ena mumpingo amafuna kutengelako, ndipo amamva bwino kuikiza miyoyo yawo yauzimu m’cisamalilo cake.—1 Akor. 11:1; 16:15, 16.
10 Abale oyenelela amenewa, amatumikila mumpingo wacikhristu pa udindo wolingana na uja wa akulu mu Isiraeli, amene anali amuna “anzelu, aluso ndi ozindikila.” (Deut. 1:13) Sikuti akulu ni anthu osacimwa ayi. Ngakhale n’conco, afunikabe kudziŵika mumpingo komanso kudela kumene akhala kuti amaopa Mulungu, ndipo aonetsa kwa nthawi yaitali kuti amayendela mfundo za Mulungu pa umoyo wawo. Kukhala kwawo opanda cifukwa cowaneneza naco, kumawapatsa ufulu wa kulankhula mumpingo.—Aroma 3:23.
-
-
Oyang’anila Oweta Nkhosa za MulunguGulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
-
-
11 Abale oikidwa kukhala oyang’anila amaonetsa kuti ni odziletsa m’zocita zawo, komanso pocita zinthu na ena. Sacita zinthu mopitilila malile. Amadziŵika kukhala acikatikati, komanso a khalidwe lodziletsa. Ucikatikati wawo umaonekela pa zinthu monga kudya, kumwa, maseŵela, makonda ake, komanso zosangalatsa. Ni acikatikatinso pa nkhani ya moŵa, kuti asanenezedwe za kuledzela kapena ucidakwa. Munthu akakhuta moŵa, sakwanitsa kudziletsa bwino-bwino, ndipo sangathe kuyang’anila zinthu zauzimu za mpingo.
12 Munthu woyenelela kukhala woyang’anila mumpingo afunikanso kukhala wadongosolo. Ndipo dongosolo limaonekela m’maonekedwe ake, pakhomo pake, komanso m’zocita zake za masiku onse. Munthu wotelo alibe cizolowezi cocedwetsa zinthu. Amaona zofunikila, ndipo amalinganiza bwino zocita. Komanso, amakonda kuyendela mfundo za umulungu.
-
-
Oyang’anila Oweta Nkhosa za MulunguGulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
-
-
14 Woyang’anila ayenelanso kukhala munthu woganiza bwino. Izi zitanthauza kukhala womvetsa zinthu, wosafulumila kuweluza. Amamvetsa bwino mfundo za Yehova, na mmene zimathandizila. Munthu woganiza bwino amalabadila malangizo na uphungu. Sakhala waciphamaso.
-
-
Oyang’anila Oweta Nkhosa za MulunguGulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
-
-
15 Paulo anakumbutsa Tito kuti woyang’anila ni munthu wokonda zabwino. Ayenela kukhala wolungama ndiponso wokhulupilika. Makhalidwe amenewa amaonekela pocita zinthu na ena, komanso posalola kupatutsidwa pa coyenela. Sagwedezeka pa cifunilo ca Yehova, ndiponso sasunthika pa miyezo yolungama. Amadziŵa kusunga cinsinsi. Amakhalanso woceleza, wodzipeleka kuthandiza ena, ndiponso alibe kaso na zinthu zake pothandiza ena.—Mac. 20:33-35.
16 Kuti atumikile bwino, woyang’anila ayenela kukhala wokhoza kuphunzitsa bwino. Malinga na zimene Paulo anauza Tito, woyang’anila ayenela ‘kugwila mwamphamvu mawu okhulupilika pamene akuphunzitsa mwaluso, kuti athe kulimbikitsa anthu ndi ciphunzitso colondola ndiponso kudzudzula otsutsa.’ (Tito 1:9) Ayenela kukhala woganiza bwino, wokhoza kufotokoza umboni, wodziŵa kuyankha otsutsa, ndiponso waluso poseŵenzetsa Malemba kuti akhutilitse ena, na kulimbikitsa cikhulupililo cawo. Woyang’anila amatha kuphunzitsa mwaluso pa nthawi yabwino komanso pa nthawi yovuta. (2 Tim. 4:2) Munthu wina akalakwa, iye amakhala woleza mtima kuti am’dzudzule modekha, kapena kuti akhutilitse munthu wokaikila, kapena kum’limbikitsa kuti acite zabwino cifukwa ca cikhulupililo. Luso lake la kuphunzitsa limaonekela pophunzitsa gulu kapena munthu aliyense payekha.
-