LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • N’ciyani Cingakuthandizeni Kuti Musaleke Kuphunzila Baibo?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
    • 5. Musalole kuti ena akuletseni kuphunzila

      Nthawi zina, anthu ena angayese kukulefulani kuti muleke kuphunzila Baibo. Onani citsanzo ca Francesco. Tambani VIDIYO, na kukambilana mafunso aya.

      VIDIYO: Tinafupidwa Cifukwa Copilila (5:22)

      Cocitika ca mu vidiyo yakuti ‘Tinafupidwa Cifukwa Copilila.’ Francesco alekena nawo anzake atawauza kuti sazicezanso nawo.
      • Mu vidiyo iyi, kodi anzake a Francesco, komanso a m’banja lake, anacita bwanji atawauza zimene anali kuphunzila?

      • Kodi kulimbikila kwake kunakhala na zotulukapo zabwino zotani?

      Ŵelengani 2 Timoteyo 2:24, 25, na kukambilana mafunso aya:

      • Kodi a m’banja mwanu komanso anzanu, amaganiza bwanji pa zimene mukuphunzila?

      • Malinga na mavesi aya, kodi mungayankhe bwanji ngati munthu wina ayesa kukuletsani kuphunzila Baibo? N’cifukwa ciyani mungayankhe conco?

  • Kodi Ena Mungawauzeko Bwanji Uthenga Wabwino?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
    • Pouzako ena uthenga wabwino, musamangoganizila zimene mufuna kukamba, muziganilanso mozikambila. Ŵelengani 2 Timoteyo 2:​24, komanso 1 Petulo 3:​15, na kukambilana mafunso aya:

      • Kodi mungaseŵenzetse bwanji mfundo zili pa mavesi aya pouzako ena za m’Baibo?

      • Ngati acibale anu ena kapena anzanu sakuvomeleza zimene mukukamba, kodi muyenela kucita ciyani? Ndipo muyenela kupewa kucita ciyani?

      • N’cifukwa ciyani ni bwino kukambilana nawo mwaulemu, m’malo mowaumiliza kuti akhulupilile zimene mukukamba?

      Wophunzila Baibo akuuzako m’bululu wake mfundo ya m’Baibo.
Mabuku a m’Cinyanja (2000-2026)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani