-
Oyang’anila Oweta Nkhosa za MulunguGulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
-
-
11 Abale oikidwa kukhala oyang’anila amaonetsa kuti ni odziletsa m’zocita zawo, komanso pocita zinthu na ena. Sacita zinthu mopitilila malile. Amadziŵika kukhala acikatikati, komanso a khalidwe lodziletsa. Ucikatikati wawo umaonekela pa zinthu monga kudya, kumwa, maseŵela, makonda ake, komanso zosangalatsa. Ni acikatikatinso pa nkhani ya moŵa, kuti asanenezedwe za kuledzela kapena ucidakwa. Munthu akakhuta moŵa, sakwanitsa kudziletsa bwino-bwino, ndipo sangathe kuyang’anila zinthu zauzimu za mpingo.
-
-
Oyang’anila Oweta Nkhosa za MulunguGulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
-
-
14 Woyang’anila ayenelanso kukhala munthu woganiza bwino. Izi zitanthauza kukhala womvetsa zinthu, wosafulumila kuweluza. Amamvetsa bwino mfundo za Yehova, na mmene zimathandizila. Munthu woganiza bwino amalabadila malangizo na uphungu. Sakhala waciphamaso.
-
-
Oyang’anila Oweta Nkhosa za MulunguGulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
-
-
15 Paulo anakumbutsa Tito kuti woyang’anila ni munthu wokonda zabwino. Ayenela kukhala wolungama ndiponso wokhulupilika. Makhalidwe amenewa amaonekela pocita zinthu na ena, komanso posalola kupatutsidwa pa coyenela. Sagwedezeka pa cifunilo ca Yehova, ndiponso sasunthika pa miyezo yolungama. Amadziŵa kusunga cinsinsi. Amakhalanso woceleza, wodzipeleka kuthandiza ena, ndiponso alibe kaso na zinthu zake pothandiza ena.—Mac. 20:33-35.
-