-
“Kumbukilani Amene Akutsogolela Pakati Panu”Gulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
-
-
N’CIFUKWA CIANI TIYENELA ‘KUKUMBUKILA AMENE AMATITSOGOLELA’?
9 Pali zifukwa zambili zokumbukilila ‘amene amatitsogolela’ na kuwakhulupilila. N’cifukwa ciani kucita izi kuli kwaphindu kwa ife? Mtumwi Paulo anakamba kuti: “Iwo amayang’anila miyoyo yanu monga anthu amene adzayankhe mlandu. Muziwamvela ndi kuwagonjela kuti agwile nchito yawo mwacimwemwe, osati modandaula, pakuti akatelo zingakhale zokuvulazani.” (Aheb. 13:17) Conco, tiyenela kumvela na kugonjela citsogozo ca awo amene amatitsogolela, cifukwa amatiyang’anila na kutiteteza mwauzimu.
10 Pa 1 Akorinto 16:14, Paulo anati: “Zonse zimene mukucita, muzicite mwacikondi.” Zigamulo zimene iwo amapanga zokhudza anthu a Mulungu, zimazikidwa pa cikondi ceni-ceni. Ponena za cikondi cimeneco, 1 Akorinto 13:4-8 imati: “Cikondi n’coleza mtima ndiponso n’cokoma mtima. Cikondi sicicita nsanje, sicidzitama, sicidzikuza, sicicita zosayenela, sicisamala zofuna zake zokha, sicikwiya. Sicisunga zifukwa. Sicikondwela ndi zosalungama, koma cimakondwela ndi coonadi. Cimakwilila zinthu zonse, cimakhulupilila zinthu zonse, cimayembekezela zinthu zonse, cimapilila zinthu zonse. Cikondi sicitha.” Inde, popeza zigamulo zawo zonse zimazikidwa pa cikondi copindulitsa atumiki a Yehova, ndife otetezeka kwambili pansi pa uyang’anilo wawo. Ndipo Yehova ndiye gwelo la cikondi cimeneci.
Tikhale ogonjela kwa aja oyang’anila umoyo wathu wauzimu
11 Monga zinalili m’nthawi ya Akhristu oyambilila, Yehova amagwilitsila nchito anthu opanda ungwilo kutsogolela gulu lake. Kuyambila kale, Yehova wakhala akugwilitsila nchito anthu opanda ungwilo kuti akwanilitse cifunilo cake. Nowa anakhoma cingalawa na kulalikila za ciwonongeko. (Gen. 6:13, 14, 22; 2 Pet. 2:5) Mose anasankhidwa kuti atsogolele anthu a Yehova kutuluka mu Iguputo. (Eks. 3:10) Amuna opanda ungwilo anauzilidwa kulemba Baibo. (2 Tim. 3:16; 2 Pet. 1:21) Sititaya cidalilo cathu pa gulu la Mulungu, ngakhale kuti Yehova amagwilitsila nchito anthu opanda ungwilo kutsogolela nchito yolalikila na kupanga ophunzila. M’malomwake, zimatilimbikitsa podziŵa kuti popanda thandizo la Yehova, gulu lathu silikanakwanitsa kucita zimene limacita. Ngakhale kuti kapolo wokhulupilikayo wapita m’mavuto ambili, iye waonetsa kuti amatsogoleledwa na mzimu wa Mulungu. Yehova wakhala akukhuthulila madalitso ake pa gawo la padziko lapansi la gulu lake. Conco, tiyeni tilicilikize gulu limeneli, komanso tilikhulupilile na mtima wonse.
-
-
“Kumbukilani Amene Akutsogolela Pakati Panu”Gulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
-
-
14 Timaonetsanso kuti timadalila gulu la Mulungu mwa kulabadila zigamulo zake. Timakhalanso odzicepetsa potsatila citsogozo ca abale oikidwa pa maudindo, monga oyang’anila madela komanso akulu mumpingo. Abalewa akuphatikizidwa pa “amene akutsogolela,” oyenela kuwamvela na kuwagonjela. (Aheb. 13:7, 17) Ngakhale tisamvetse zifukwa zonse zopangila zigamulo zina zake, timadziŵa kuti kulabadilabe kuli na ubwino wake kwa ife. Zotulukapo n’zakuti Yehova amatidalitsa pomvela Mawu ake na gulu lake. Tikatelo, timaonetsanso kuti timagonjela Mbuye wathu, Yesu Khristu.
-