-
Tsanzilani Cikhulupililo ca MoseNsanja ya Mlonda—2014 | April 1
-
-
1, 2. (a) Kodi Mose anapanga cosankha cotani ali ndi zaka 40? (Onani cithunzi cili kuciyambi kwa nkhani ino.) (b) N’cifukwa ciani Mose anasankha kuzunzidwa pamodzi ndi anthu a Mulungu?
MOSE anadziŵa kuti akanakhala ndi tsogolo labwino m’dziko la Iguputo. Dzikolo linali ndi nyumba zazikulu zokongola ndipo linali lotukuka. Iye anakulila m’banja lacifumu ndipo “anaphunzila nzelu zonse za Aiguputo.” Mwacionekele, iye anaphunzila luso losiyanasiyana, zinthu zakuthambo, masamu, ndi sayansi. (Mac. 7:22) Zikanakhala zosavuta kuti iye akhale ndi cuma, ulamulilo ndi udindo, zinthu zimene Aiguputo ena sakanakhala nazo.
2 Komabe, ali ndi zaka 40, Mose anapanga cosankha cimene cinadabwitsa banja lacifumu laciiguputo limene linali kum’sunga. Iye sanasankhe ngakhale umoyo wa Aiguputo wamba, koma anasankha kukhala pamodzi ndi akapolo. N’cifukwa ciani anasankha zimenezo? Cifukwa cakuti Mose anali ndi cikhulupililo. (Ŵelengani Aheberi 11:24-26.) Cifukwa ca cikhulupililo, Mose sanaike maganizo ake pa zinthu zooneka ndi maso. Iye anali kukhulupililabe “Wosaonekayo,” Yehova, ndi malonjezo ake.—Aheb. 11:27.
-
-
Tsanzilani Cikhulupililo ca MoseNsanja ya Mlonda—2014 | April 1
-
-
6. (a) N’cifukwa ciani Mose anakana “kuchedwa mwana wa mwana wamkazi wa Farao”? (b) N’cifukwa ciani tinganene kuti Mose anasankha zinthu mwanzelu?
6 Cikhulupililo cinathandizanso Mose kusankha zocita paumoyo. “Mwa cikhulupililo, Mose atakula anakana kuchedwa mwana wa mwana wamkazi wa Farao.” (Aheb. 11:24) Mose sanaganize kuti angatumikile Mulungu m’nyumba yacifumu ndi kugwilitsila nchito cuma cake kuthandiza abale ake Aisiraeli. M’malo mwake, anatsimikiza mtima kukonda Yehova ndi mtima wake wonse, moyo wake wonse ndi mphamvu zake zonse. (Deut. 6:5) Zimene Mose anasankha zinam’thandiza kupewa mavuto aakulu. Cuma cambili ca Aiguputo cimene anakana cinafunkhidwa ndi Aisiraeli. (Eks. 12:35, 36) Farao anacititsidwa manyazi ndipo anaphedwa. (Sal. 136:15) Koma Mose anapulumutsidwa ndipo Mulungu anam’gwilitsila nchito kutsogolela Aisiraeli kuti apulumuke. Ndithudi, moyo wake unali waphindu.
-