-
Kodi Mumaona “Wosaonekayo”?Nsanja ya Mlonda—2014 | April 1
-
-
10. (a) Kodi Yehova anapeleka malangizo otani kwa Aisiraeli m’mwezi wa Nisani mu 1513 B.C.E.? (b) N’cifukwa ciani Mose anamvela malangizo a Mulungu?
10 M’mwezi wa Nisani m’caka ca 1513 B.C.E., Yehova anatuma Mose ndi Aroni kukapeleka malangizo awa kwa Aisiraeli: Sankhani nkhosa yaimuna kapena mbuzi yopanda cilema, muiphe ndi kuwaza magazi ake pamakomo a nyumba zanu. (Eks. 12:3-7) Kodi Mose anacita ciani? Patapita zaka zambili, mtumwi Paulo analemba izi ponena za iye: “Mwa cikhulupililo, iye anacita pasika ndiponso anawaza magazi pamafelemu a pakhomo, kuti woonongayo asakhudze ana ao oyamba kubadwa.” (Aheb. 11:28) Mose anadziŵa kuti Yehova ndi wokhulupilika, ndipo anakhulupilila lonjezo la Yehova lakuti adzapha ana aamuna oyamba kubadwa aciiguputo.
11. N’cifukwa ciani Mose anapeleka malangizo kwa Aisiraeli?
11 Mose anali kuwakonda Aisiraeli. Ngakhale kuti ana ake aamuna anali otetezeka ndipo anali kutali ku Midiyani, iye anapeleka malangizo ku mabanja aciisiraeli amene ana ao aamuna anali pa ngozi. (Eks. 18:1-6) Kuti awateteze kwa “woonongayo,” mwamsanga Mose “anaitana akulu onse a Isiraeli ndi kuwauza kuti: . . . ‘Muiphele nsembe ya pasika.’”—Eks. 12:21.a
12. Ndi uthenga wofunika uti umene Yehova watituma kukalengeza?
12 Anthu a Yehova akuthandizidwa ndi angelo kulengeza uthenga wofunika wakuti: “Opani Mulungu ndi kumupatsa ulemelelo, cifukwa ola lakuti apeleke ciweluzo lafika. Cotelo lambilani Iye amene anapanga kumwamba, dziko lapansi, nyanja, ndi akasupe amadzi.” (Chiv. 14:7) Ino ndiyo nthawi yolengeza uthenga umenewo. Tifunika kucenjeza anansi athu kuti atuluke m’Babulo Wamkulu kotelo kuti ‘asalandileko ina ya milili yake.’ (Chiv. 18:4) A “nkhosa zina” akuthandiza Akristu odzozedwa kupempha anthu otalikilana ndi Mulungu kuti ‘agwilizanenso’ ndi iye.—Yoh. 10:16; 2 Akor. 5:20.
13. N’ciani cidzatithandiza kukhala wofunitsitsa kulalikila uthenga wabwino?
13 Ndife otsimikiza kuti “nthawi ya ciweluzo” yafika. Ndiponso, ndife otsimikiza mtima kugwila nchito yolalikila mwamsanga monga mmene Yehova akufunila. Mtumwi Yohane anaona masomphenya a “angelo anai ataimilila m’makona anai a dziko lapansi. Iwo anali atagwila mwamphamvu mphepo zinai za dziko lapansi.” (Chiv. 7:1) Ndi maso a cikhulupililo, kodi mumaona angelo amenewo kuti atsala pang’ono kusiya kugwila mphepo zoononga za cisautso cacikulu padziko lapansi? Pitilizani kukhulupilila malonjezo a Yehova. Kucita zimenezi kudzakuthandizani kukhala wofunitsitsa kulalikila uthenga wabwino.
-
-
Kodi Mumaona “Wosaonekayo”?Nsanja ya Mlonda—2014 | April 1
-
-
a Yehova anatumiza angelo kukapha ana aamuna oyamba kubadwa aciiguputo.—Sal. 78:49-51.
-