LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • ypq funso 7 masa. 21-23
  • Ningacite Bwanji Ngati Wina Aninyengelela kuti Nigone Naye?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Ningacite Bwanji Ngati Wina Aninyengelela kuti Nigone Naye?
  • Mayankho pa Mafunso 10 Amene Acicepele Amafunsa
Mayankho pa Mafunso 10 Amene Acicepele Amafunsa
ypq funso 7 masa. 21-23
Mtsikana akanilatu pamene mnyamata ayesa kum’funa

7

Ningacite Bwanji Ngati Wina Aninyengelela kuti Nigone Naye?

CIFUKWA CAKE UFUNIKA KUDZIŴA

Zimene ungasankhe kucita pa nkhani ya kugonana zikhoza kukhudza umoyo wako wonse.

KUKHALA IWE UNGACITE BWANJI?

Ganizila cocitika ici: Ngakhale kuti Heather wakhala akuceza na Mike kwa miyezi iŵili cabe, amvela monga anadziŵana naye kalekale. Iwo amatumizilana mameseji na kuceza nthawi itali pafoni, cakuti afika pokondana kwambili! Koma manje, Mike afuna zipitilile pa kuceza cabe.

M’miyezi iŵili imeneyi, Mike na Heather akhalanso akugwilana manja na kukising’ana pang’ono. Ngakhale kuti Heather safuna kuti zipitilile apa, safunanso kuti cibwenzi cawo cisile. Ndipo amakamba mumtima mwake kuti ‘Koma Mike na ine tikondana . . . ’

Kukhala Heather, kodi ungacite bwanji?

YAMBA WAIMA NA KUGANIZA!

Apukutila covala cokongola

Kugonana ni mphatso yocokela kwa Mulungu kwa anthu ali m’cikwati. Koma kugonana mukalibe kungena m’cikwati, kumakhala monga kutenga cinthu ca mtengo wapatali n’kuciviika m’zinthu zonyansa. Cilinso monga kutenga covala cokongola cimene wina anakugulila n’kuyamba kucipukutila.

Ngati upitilila dala maloboti akayaka redi, umadzibweletsela mavuto. Ndiye mmene zimakhalila ukaphwanya yamulo ya m’Baibo monga yakuti: ‘Pewani dama.’—1 Atesalonika 4:3.

Ni mavuto anji amene amabwela ukaphwanya lamulo imeneyi? Baibo imati: “Amene amacita dama amacimwila thupi lake.” (1 Akorinto 6:18) Nanga zimacitika bwanji?

Ofufuza apeza kuti acicepele ambili amene anagona na munthu wina akalibe kungena m’banja amakumana na mavuto aya.

  • KUVUTIKA MAGANIZO. Acicepele ambili amene amagona na munthu wina akalibe kungena m’banja amadziimba mlandu pambuyo pake.

  • KUSAKHULUPILILANA. Pambuyo pakuti anthu aŵili agonana, onse aŵili amayamba kuda nkhawa na kudzifunsa kuti, ‘kodi ameneyu wagonapo na ine cabe?’

  • KUDZIGONG’A. Pansi pamtima, atsikana ambili amafuna mnyamata amene angawateteze, osati amene amafuna kuwaseŵenzetsa cabe. Ndipo anyamata ambili sapitiliza kukonda mtsikana amene anavomela kucita nawo ciwelewele.

  • Zimene ufunika kudziŵa: Ukagona na munthu ukalibe kungena m’cikwati, udziŵe kuti wadzichipitsa mwa kupangitsa thupi yako kukhala conyansa. (Aroma 1:24) Thupi yako ni yamtengo wapatali kwambili. Si cinthu coseŵeletsa!

Onetsa kuti munthu sangakuchipitse. Ungacite zimenezi mwa “kupewa dama.” (1 Atesalonika 4:3) Koma pamene udzangena m’cikwati, kugonana kudzakhala mphatso yokondweletsa kwambili. Mudzayamba kugonana popanda nkhawa iliyonse, kudziimba mlandu, kapena zotulukapo zoipa zimene zimabwela cifukwa cogonana mukalibe kuloŵa m’cikwati.—Miyambo 7:22, 23; 1 Akorinto 7:3.

UGANIZA BWANJI?

  • Kodi munthu amene amakukonda zoona, angakupangitse kucita cinthu cimene cingakubweletsele mavuto pambuyo pake?

  • Kodi munthu amene amakukonda zoona, angafune kukuwonongela unansi wako na Mulungu?—Aheberi 13:4.

MTSIKANA, DZIŴA IZI

Mtsikana wakhala pansi aganiza

Anyamata ambili amakamba kuti sangakwatile mtsikana amene anagonapo naye. Cifukwa ciani? Cifukwa amafuna kukwatila mtsikana amene amadzisunga.

Kodi zimenezi zakudabwitsa—kapena zakukwiitsa? Ndipo kumbukila izi: Mafilimu na mapulogilamu ena a pa TV amalimbikitsa acicepele kumagonana. Amaonetsa kuti ni cinthu cabwino, cokondweletsa, ndipo amati n’cikondi ceni-ceni.

Koma asakupusitse! Amene angayese kukunyengelela kuti ugone nawo angofuna kukhutilitsa zofuna zawo zadyela.—1 Akorinto 13:4, 5.

MNYAMATA, DZIŴA IZI

Mnyamata wakhala pansi aganiza

Ngati uli pa cibwenzi na mtsikana, dzifunse kuti, ‘Kodi nimam’konda zoona?’ Ngati uyankha kuti inde, ungaonetse bwanji zimenezo? Mwa kusunga malamulo a Mulungu, kupewa macitidwe amene angabweletse ciyeso, na kum’funila zabwino.

Ngati una makhalidwe amenewa, mtsikana wako adzamvela monga mmene msulami, mtsikana wa makhalidwe abwino, anamvelela. Iye anacita kukamba kuti: “Wacikondi wanga ndi wanga, ndipo ine ndine wake.” (Nyimbo ya Solomo 2:16) Mwacidule, cikondi cake pa iwe cidzakulilatu!

TIKUPATSEKO NZELU

Nzelu yoyamba: Ngati munthu wina ayesa kukunyengelela kuti ugone naye pokuuza kuti, “Ngati unikonda, udzavomela,” uyenela kukana mosapita m’mbali kuti, “Ngati unikonda, sunganipemphe kuti ticite zimenezi!”

Nzelu yaciŵili: Pocita zinthu na munthu amene uli naye pacibwenzi, uziyendela lamulo iyi: Ngati ni cinthu cimene makolo ako sangakulole kucita, usacicite.

ZOFUNIKA KUCITA

  • Ungayankhe bwanji ngati munthu wina akupempha kuti ugone naye?

  • Kodi n‘zocitika ziti zingapangitse kuti uvutike kukana?

  • Nanga ungazipewe bwanji zocitika zimenezo?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani