LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w25 May tsa. 32
  • Konzekeletsani Mtima Wanu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Konzekeletsani Mtima Wanu
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
  • Nkhani Zofanana
  • Kunola Luso Lathu mu Ulaliki Kuthandiza Maphunzilo Athu a Baibo Kukonzekela
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
  • Tetezani Mtima Wanu
    Imbirani Yehova
  • Mfundo Yothandiza pa Kuŵelenga Kwanu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2024
  • Ezara Aphunzitsa Cilamulo ca Mulungu
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
w25 May tsa. 32

MFUNDO YOTHANDIZA PA KUWELENGA KWANU

Konzekeletsani Mtima Wanu

Pamene tiwelenga Baibo, timafuna kuti kaganizidwe ka Yehova kakhudze mtima komanso umunthu wathu wamkati. Ezara anapeleka citsanzo cabwino pamene “anakonzekeletsa mtima wake kuti aphunzile Cilamulo ca Yehova.” (Ezara 7:10) Kodi tingaukonzekeletse motani mtima wathu?

Pemphelani. Mukalibe kuyamba kuwelenga, muzipemphela. M’pempheni Yehova kuti akuthandizeni kumvetsa komanso kugwilitsa nchito zimene mufuna kuphunzila.​—Sal. 119:​18, 34.

Khalani wodzicepetsa. Mulungu amabisa coonadi cake kwa anthu amene modzikuza amadalila nzelu zawo. (Luka 10:21) Pamene tikuwelenga, colinga cathu cisamakhale kufuna kudzionetsela kwa ena kuti tidziwa zambili. Modzicepetsa, sinthani kaganizidwe kanu ngati sikagwilizana ndi kaganizidwe ka Mulungu.

Mvetselani nyimbo ya Ufumu. Nyimbo zili ndi mphamvu yokhudza mtima wathu. Conco kumvetsela nyimbo ya Ufumu tisanayambe kuwelenga kungatithandize kuika maganizo athu pa Yehova kuti zimene tidzaphunzila zitifike pamtima.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani