-
Numeri 25:17, 18Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
17 “Akhaulitseni Amidiyani ndipo muwaphe,+ 18 chifukwa akubweretserani tsoka mochenjera pokukopani kuti muchimwe ku Peori.+ Muwaphe ndithu, chifukwanso cha zochita za mchemwali wawo Kozibi, mwana wa mtsogoleri wa ku Midiyani, amene anaphedwa+ pa tsiku limene mliri unakugwerani chifukwa cha zimene zinachitika ku Peori.”+
-
-
Deuteronomo 4:3Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
3 Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita pa nkhani ya Baala wa ku Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga pakati panu munthu aliyense amene anatsatira Baala wa ku Peori.+
-
-
Yoswa 22:17Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
17 Kodi zoipa zimene tinachita ku Peori zatichepera? Sitinadziyeretsebe ku tchimo limene lija mpaka lero, ngakhale kuti mliri unagwera anthu a Yehova.+
-