Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • Levitiko 26:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 ndidzakugwetserani mvula pa nthawi yake.+ Nthaka idzakupatsani chakudya,+ ndipo mitengo yamʼmunda idzakupatsani zipatso zake.

  • Deuteronomo 8:7-9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Chifukwa Yehova Mulungu wanu akukulowetsani mʼdziko labwino,+ dziko la mitsinje ya madzi,* akasupe ndi madzi ochuluka amene akuyenda mʼzigwa ndi mʼdera lamapiri, 8 dziko la tirigu, balere, mphesa, mitengo ya mkuyu ndi makangaza,*+ dziko la maolivi opangira mafuta ndiponso la uchi,+ 9 mʼdziko limene simudzasowa chakudya komanso simudzasowa chilichonse, dziko limene miyala yake amapangira zitsulo, limenenso mʼmapiri ake mudzakumbamo kopa.*

  • Deuteronomo 28:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Yehova adzakutsegulirani kumwamba, nyumba yake yabwino yosungiramo zinthu, kuti akupatseni mvula pa nyengo yake+ mʼdziko lanu ndi kudalitsa chilichonse chimene mukuchita. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inuyo simudzafunika kukongola kanthu kwa iwo.+

  • Yeremiya 14:22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Kodi pa mafano opanda pake a mitundu ya anthu pali fano lililonse limene lingagwetse mvula?

      Kapena kodi kumwamba pakokha kungagwetse mvula yamvumbi?

      Kodi si inu nokha, Yehova Mulungu wathu, amene mumachititsa zimenezi?+

      Chiyembekezo chathu chili mwa inu

      Chifukwa inu nokha ndi amene mumachita zonsezi.

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani