-
Yoswa 9:1, 2Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
9 Mafumu onse amene anali kumadzulo kwa Yorodano+ anamva zimene zinachitika. Amenewa anali mafumu a Ahiti, Aamori, Akanani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.+ Iwo ankakhala kudera lamapiri, ku Sefela ndiponso mʼmbali monse mwa Nyanja Yaikulu*+ komanso pafupi ndi Lebanoni. Mafumuwa atangomva zimene zinachitikazo, 2 anapanga mgwirizano kuti amenyane ndi Yoswa ndi Isiraeli.+
-