Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • 1 Mafumu 8:14-21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Kenako mfumu inatembenuka nʼkuyamba kudalitsa gulu lonse la Aisiraeli. Apa nʼkuti Aisiraeli onsewo ataimirira.+ 15 Mfumuyo inati: “Atamandike Yehova Mulungu wa Isiraeli, amene ndi pakamwa pake analonjeza bambo anga Davide ndipo ndi dzanja lake wakwaniritsa zimene ananena zakuti, 16 ‘Kuyambira tsiku limene ndinatulutsa anthu anga Aisiraeli mʼdziko la Iguputo, sindinasankhe mzinda mʼmafuko onse a Isiraeli womangako nyumba ya dzina langa kuti likhale kumeneko.+ Koma ndasankha Davide kuti alamulire anthu anga Aisiraeli.’ 17 Ndipo bambo anga Davide ankafunitsitsa kumanga nyumba ya dzina la Yehova Mulungu wa Isiraeli.+ 18 Koma Yehova anauza Davide bambo anga kuti, ‘Unkafunitsitsa kumanga nyumba ya dzina langa ndipo unachita bwino kulakalaka utachita zimenezi. 19 Koma iweyo sumanga nyumbayi, mʼmalomwake mwana wamwamuna amene udzabereke* ndi amene adzamange nyumba ya dzina langa.’+ 20 Yehova wakwaniritsa zimene analonjeza, chifukwa ndalowa mʼmalo mwa bambo anga Davide ndipo ndakhala pampando wachifumu wa Isiraeli, mogwirizana ndi zimene Yehova analonjeza. Komanso ndamanga nyumba ya dzina la Yehova Mulungu wa Isiraeli.+ 21 Ndiponso mʼnyumbamo ndakonzamo malo oika Likasa, lomwe muli pangano+ limene Yehova anapangana ndi makolo athu pamene ankawachotsa mʼdziko la Iguputo.”

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani