-
1 Mafumu 8:41-43Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
41 Komanso mlendo amene si mmodzi wa anthu anu Aisiraeli, amene wabwera kuchokera kudziko lakutali chifukwa cha dzina lanu*+ 42 (popeza adzamva za dzina lanu lalikulu,+ dzanja lanu lamphamvu ndiponso mkono wanu wokonzeka kuthandiza*), ndipo wabwera nʼkupemphera atayangʼana nyumbayi, 43 inuyo mumve muli kumwambako, kumene mumakhala,+ ndipo muchite zonse zimene mlendoyo wakupemphani. Muchite zimenezi kuti anthu a mitundu yonse yapadziko lapansi adziwe dzina lanu ndiponso akuopeni+ ngati mmene anthu anu Aisiraeli amachitira, komanso adziwe kuti dzina lanu lili panyumba imene ndamangayi.
-