17 Ndiyeno ndinaganizira ntchito yonse ya Mulungu woona, ndipo ndinazindikira kuti anthu sangamvetse zimene zimachitika padziko lapansi pano.+ Ngakhale anthu atayesetsa bwanji sangathe kuzimvetsa. Ngakhale atanena kuti ndi anzeru kwambiri ndipo zonsezi akuzidziwa, sangathebe kuzimvetsa.+