29 Kodi madzi oundana amachokera mʼmimba mwa ndani,
Ndipo ndi ndani amene anabereka nkhungu yamumlengalenga?+
30 Kodi ndi ndani amene amachititsa chivundikiro cha madzi kuti chikhale cholimba ngati mwala,
Komanso kuti madzi amene ali pamwamba pa madzi akuya aundane chifukwa chozizira?+