11 Chifukwa mofanana ndi dziko lapansi limene limatulutsa zomera zake,
Ndiponso mofanana ndi munda umene umameretsa zinthu zimene zadzalidwa mmenemo,
Nayenso Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa,
Adzachititsa kuti chilungamo+ komanso mawu otamanda zimere+ pamaso pa mitundu yonse.