Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • Salimo 38:22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Bwerani mwamsanga mudzandithandize,

      Inu Yehova, amene mumandipulumutsa.+

  • Salimo 70:1-5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 70 Inu Mulungu, ndipulumutseni,

      Inu Yehova, ndithandizeni mofulumira.+

       2 Amene akufuna kuchotsa moyo wanga

      Achititsidwe manyazi komanso anyozeke.

      Amene akusangalala ndi tsoka langa

      Abwerere mwamanyazi.

       3 Onse amene akunena kuti: “Eyaa! Eyaa!”

      Abwezedwe mwamanyazi.

       4 Koma amene akufunafuna inu,

      Akondwere ndi kusangalala chifukwa choti akudziwani.+

      Amene amasangalala ndi njira imene mumapulumutsira anthu, nthawi zonse azinena kuti:

      “Mulungu alemekezeke.”

       5 Koma ine ndine munthu wovutika komanso wosauka.+

      Inu Mulungu, ndithandizeni mwamsanga.+

      Inu ndi amene mumandithandiza komanso kundipulumutsa.+

      Inu Yehova musachedwe.+

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani