Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • 2 Mbiri 36:22, 23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Mʼchaka choyamba cha Koresi+ mfumu ya Perisiya, pokwaniritsa mawu a Yehova amene analankhula kudzera mwa Yeremiya,+ Yehova analimbikitsa Koresi mfumu ya Perisiya kuti alengeze mu ufumu wake wonse, zomwenso iye analemba mʼmakalata,+ kuti: 23 “Koresi mfumu ya Perisiya wanena kuti, ‘Yehova Mulungu wakumwamba wandipatsa maufumu onse apadziko lapansi.+ Iye wandituma kuti ndimumangire nyumba ku Yerusalemu mʼdziko la Yuda.+ Aliyense amene ali pakati panu mwa anthu onse amene amamutumikira, Yehova Mulungu wake akhale naye ndipo apite.’”+

  • Ezara 6:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 “Mʼchaka choyamba cha Mfumu Koresi, mfumuyo inaika lamulo lokhudza nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu lakuti:+ ‘Ayuda amangenso nyumbayo kuti azikapereka nsembe kumeneko ndipo amange maziko olimba. Nyumbayo ikhale mikono 60* kupita mʼmwamba ndiponso mikono 60 mulifupi mwake.+

  • Yesaya 45:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Ine ndapatsa munthu mphamvu kuti achitepo kanthu mwachilungamo,+

      Ndipo njira zake zonse ndidzaziwongola.

      Iye ndi amene adzamange mzinda wanga+

      Komanso kumasula anthu anga amene ali ku ukapolo,+ popanda malipiro kapena chiphuphu,”+ akutero Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani