Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • 2 Mbiri 36:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Choncho anawabweretsera mfumu ya Akasidi+ yomwe inapha anyamata awo ndi lupanga+ mʼnyumba yopatulika.+ Sinamvere chisoni mnyamata kapena namwali, wachikulire kapena wodwala.+ Mulungu anapereka zonse mʼmanja mwake.+

  • Yeremiya 51:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  7 Babulo anali ngati kapu yagolide mʼdzanja la Yehova.

      Anachititsa kuti dziko lonse lapansi liledzere.

      Mitundu ya anthu yaledzera ndi vinyo wake.+

      Nʼchifukwa chake mitundu ya anthu ikuchita zinthu ngati anthu amisala.+

  • Ezekieli 29:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Choncho Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti, ‘Ine ndikupereka dziko la Iguputo kwa Nebukadinezara* mfumu ya Babulo.+ Iye adzatenga chuma cha dzikolo komanso kulanda zinthu zake zochuluka. Zimenezi zidzakhala malipiro a asilikali ake.

  • Danieli 5:18, 19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Inu mfumu, Mulungu Wamʼmwambamwamba anapatsa bambo anu Nebukadinezara ufumu, ukulu, ulemu ndi ulemerero.+ 19 Chifukwa chakuti Mulungu anamupatsa ukulu umenewu, anthu a mitundu yonse komanso anthu olankhula zinenero zosiyanasiyana ankanjenjemera chifukwa cha mantha pamaso pake.+ Aliyense amene ankafuna kumupha ankamupha, amene ankafuna kumusiya ndi moyo ankamusiya ndipo aliyense amene ankafuna kumukweza ankamukweza, amene ankafuna kumutsitsa ankamutsitsa.+

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani